Psalms 131

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,
maso anga siwonyada;
sinditengeteka mtima
ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
2Koma moyo wanga ndawutontholetsa
ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,
moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.

3Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Copyright information for NyaCCL